Typhoid fever (kamwazi) ndi matenda omwe a Malawi ambiri
akuwadziwa. Matendawa, omwe nthawi zina anthu amasokoneza ndi malungo chifukwa
chofanana zizindikiro, timayambitsa ndi tizirombo totchedwa bakiteria.
Matenda a kamwazi amayambitsa kutsegula m’mimba ndi ziwengo, kamba
ka mtundu wa bakiteria womwe umayambitsa matendawa wa Salmonella typhi (S.
typhi).
Nanga matendawa amayamba bwanji ndipo tingawapewe bwanji?
Ka chilombo ka S. typhi kamafala kudzela mu zakudya, zakumwa komanso
madzi amene mwapezeka tizilomboti. Ngati mwadya kapena kumwa madzi omwe muli
tizilombo toyambitsa kamwazi, tizilomboti timalowa mthupi mwanu kudzera mu
matumbo. Kenako tizilomboti timachoka mu matumbo ndikulowa mu magazi momwe
timafala ku ziwalo zosiyana siyana.
Kuopsya kwa matendawa
ndi koti anthu ena amatha kukhala ndi matendawa mthupi mwao koma osadwala.
Anthu oterewa amatchewa “afalitsi” (pa chizungu amati ma carriers), anthuwa
amanka na falitsa matendawa asakudziwa. Anthuwa amafalitsa matendawa kudzera mu
chimbudzi chawo, ndipo akhoza kufalitsa matendawa kwa zaka zambiri.
Zizindikiro za matendawa
Chizikiro choyamba ndi kutentha
kwa mthupi, kuphwanya mthupi ndi kupweteka kwa m’mimba, ndi kutegula m’mimba.
Anthu ena amakhala ndi ziwengo zomwe zimaoneka ngati madontho
ofira pa mimba ndi pa chifuwa.
Matendawa ndi oopsya choncho ndi chofunikira kuti ngati mwaona
zizindikilozi, mupite ku chitala mwa msanga kuti mukalandire chithandizo.
Musayiwale kuti kamwazi ndi nthenda ya chisanu ndi chinayi (9) yoopsa
pa dziko lonse lapansi pa matenda opatsirana.
No comments:
Post a Comment