Ngakhale njira zilipo
zopewera matendawa, komanso kupezeka kwa mankhwala osiyana siyana ochiza ena
mwa matendawa, vutoli lidakalipobe.
Chifukwa chain vutoli la matendawa
lidakalipobe?
Yankho kapena nditi
mayankho alipo angapo, ena mwa iwo ndi awa;
1. Anthu ambiri sadziwa kuti matendawa tikhoza ku wapewa
2. Anthu ambiri sakudziwa njira zopewera matendawa
3. Kusowa kwa mankhwala omwe amathandiza ku chepetsa komanso
kuchiza matendawa
4. Kuchepa kwa maphunziro, choncho anthu ambiri satha kuwerenga ndi
kulemba ndipo sangathe kuwerenga za njira zopewera kapena kupeza chithandizo
ku matendawa.
5. Ku kwera mtengo kwa mankhwala komanso zipatala zolipira komwe
anthu angathe kupeza ena mwa mankhwala oti angawathandize ku matendawa
6. Umphawi womwe umapangitsa anthu kukhala m’malo komanso kumwa
madzi ndi kudya zakudya zoti si za ukhondo
Nanga tingathandizane
bwanji kuti tichepetse kapena kupewa kumene matenda opatsiranawa?
Chifukwa cha kuopsya
kwa matenda opatsirana, maiko osiyana siyana pa dziko lonse anagwirizana pa
mfundo yotchedwa “Millenium Development goals” omwe pa Chichewa tinganti
“Mfundo za chitukuko muchilimika cha mileniyamu”. Imodzi mwa mfundo zomwe
anagwirizana ndi :
Kuthetsa komanso
kutembenuza njira za kufala kwa matenda opatsirana pofika chaka cha 2015.
Kodi maiko wa
akwaniritsa bwanji mfundo imeneyi?
Ilitu ndi funso lomwe
dziko lili lonse liyenera kuyankha. Maiko osiyana siyana akonza njira zomwe
akutsata kuti athane ndi vuto la matenda opatsiranawa. Zina mwa njirazi ndi;
1) Kuonetsetsa kuti anthu
aphunzitsidwe njira zopewera matenda opatsirana
2) Kuonetsetsa kuti anthu
akulandira mankhwala oyenerera ochepetsa komanso ku chiza matendawa
3) Kuonesetsa kuti anthu ali
ndi madzi a ukhondo komanso akuphunzitsidwa njira zosiyana siyana za ukhondo.
Chikhazikitsileni mfundo
za chitukukuko mu chilimika cha mileniyamu mu chaka cha 2000, zina mwa zinthu
zomwe maiko akwaniritsa ndi;
· Kuchepetsa kwa imfa chifukwa cha matenda a chikuku ndi pafupi
fupi 92% mu Africa ndi Madera a ku mvuma kwa Nyanja ya Mediterenian (East
Medeterenian)
· Pafupifupi kuthetsa matenda a Polio ndi matenda ena opatsirana kudzera mu tinyongolotsi (worm diseases)
Izi ndi zina mwazitsanzo za njira zomwe maiko akuyesetsa kukhazikitsa mu kulimbana ndi matenda opatsirana.
No comments:
Post a Comment